Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 169

Miyambi ya Patsokwe Mwala wogubuduzika sumera ndere. -Kusakhazikika pamalo kapena pantchito kumachititsa kuti tisapeze mwayi. Mwala woyendayenda suyanga ndere. -Kusakhazikika pamalo kapena pantchito kumachititsa kuti tisapeze mwayi. Mwalemera nyanga yanga simuidya. -Munthu ukazolowera moyo wofewa mavuto suwaganizira. Mwamuna koma kumuyang’ana kumimba. -Mayi amayenera kudziwa kuti kuti mwamuna agwire ntchito bwino amafunika kumupatsa chakudya. Mwamuna mnzako mpachulu, umalinga utakwerapo. -Osamaderera mnzako usanaone mphamvu zake, chifukwa nthawi zina wonyozeka m’maso ndi amene amakutidzimula kapena kukuposa pa chinachake. Mwamuna mpamimba, nkhope siisintha. -Mayi amayenera kudziwa kuti pakhomo kuti mwamuna agwire ntchito bwino amafunika kumupatsa chakudya. Mwamuna ndi kabudula, amathera moyenda. -Mwamuna sakulira malo amodzi. Amafunika kuyendayenda kuti akasake ndalama zothandizira mkazi komanso abale ake. Mwamuna ndine ndekha adam’pachika ndi mkuzi. -Osamadzikuza chifukwa ena akhoza kutichititsa manyazi ife n’kunyowa. Mwana akalilira fupa m’ninkhe. -Nthawi zina ndi bwino kumalolera kuti ana achite zofuna zawo. Ndi bwino kumaloleza maganizo kapena zimene anthu ena akufuna kuti aphunzirepo kathu. 168