Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 168

Miyambi ya Patsokwe Mvula yamvumbi kunyenga ana. -Si bwino kutengeka ndi zinthu zomwe zimaoneka ngati si zoipa kwenikweni. Zinthu ngati zimenezi zimachititsa kuti tidziimbe mlandu kapena tikumane ndi mavuto ngati mmene mwana amene wanyowa kapena wadzidetsa ndi matope a mvumbi amachitira. Mvumbi kwa ana, akulu nadya nthanga. -Mawuwa amadzudzula khalidwe lodzikonda. Mwachitsanzo, makolo kumadya kapena kumapeza zabwino ana ali pamvumbi, kapena akuvutika. Mvuu zikatha, amakankha bwato ndi kampango. -Mavuto satherapo, akatha awa amabweranso ena. Mwa limodzi anaonera khumi kutha. -Nthawi zina mukagwira wakuba m’modzi amatha kuulula anzake ambiri. Mwachaje satafuna. -Munthu sangatafune m’kamwa mopanda kanthu. Munthu wina akamadandaula ndiye kuti pali vuto, tiyenera kumumvetsera. Mwachaje satafuna. -Ndi bwino kumakhutitsidwa ndi zimene uli nazo ngakhale zili zochepa. Mwakumbakumba mbewa mwalema, m’sakadandaule ndiwo. -Munthu uyenera kuvomereza zotsatira za ntchito yako. Mwachitsanzo, mbewa zikakukanika kukumba umasowa ndiwo n’kuswera nayo njala. Mwala umene amisili aukana umasanduka wapangodya. -Nthawi zina zinthu zimene tikuziona kuti n’zosafunika zima- khala zothandiza kwambiri. 167