Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 77

Matigari Obwera ankhanza inu, Longedzani katundu wanu muone nsanawanjira! Popeza eni nyumba, akubwera kudzalowa m’nyumbayi! “Atangomva nyimbo imeneyi, mtsamunda uja anathamangi- ra pamene panali lamya. Ndipo ine ndinathamangira pamene ankasunga mfuti yake . . . Koma kunena zoona padziko lapansi pano palibenso chinthu china choipa kwambiri kuposa ukapolo. Ukapolo ndilibe nawo mawu, ndi kanyama kachabe. Ukapolo ukaphatikizana ndi umbuli umakhala nsakanizo wachabe. Umamanga maganizo komanso moyo wamunthu n’kumusiyira chibaza! Kodi ukuganiza kuti ndi ndani amene anakuwa ku- chenjeza Mtsamunda Williams? Nanga ukuganiza kuti ndi nda- ni amene anandilumphira n’kundigwira komanso kunditayitsa mfuti pamene ndinkafuna kusuntha chala changa kuti ndit- somphole chopolopolo chikalase Mtsamunda Williams? Uku- ganiza kuti angakhalenso ndani kuposa John boy!” “Boy? Wati John Boy? Ukumudziwanso munthu ameneyu?” munthu wakuda uja anafunsa mosonyeza kuti wadzidzimuka ndi zimene anamvazo. “Ndi ndani m’dziko muno amene sadziwa John Boy? Anali khukhi wa Mtsamunda Williams. Koma munthu amene uja anali wadyera komanso anali wonenepa zedi. Anali wonenepa ngati nkhumba. Iyayi, mwinanso ndachepetsa, anali wonenepa ngati mvuu! Komano munthu angayembekezere zotani kwa munthu yemwe ankangokhalira kutolera zakudya zotsala patebulo la Mtsamunda Williams—?” Thya! Thya! Matigari anamva ngati thupi lake lang’ambika. Ndipo 76