Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 76

Matigari “Mwalasa ndithu, ndi yemweyo.” “Nanenso ndinamvapo za iye. Kodi nawenso ukumudziwa? Ukudziwa zotani zokhudza mzungu ameneyu?” “Ndikudziwa zotani zokhudza mzungu ameneyu? Zoona ineyo ndisadziwe mzungu yemwe ankakolola pamene sanalime uja? Ndingaiwale bwanji mzungu amene uja, ine munthu wogwira ntchito, kuiwala mzungu yemwe ankakonda kuchita masewera a wachiona ndani? Ndiye ukuganiza kuti chinachititsa kuti tiyambe kulimbana n’chiyani? Chinali chifu- kwa choti ndinatulukira umambala wake wonse. Ndithu ndina- bwera komwekuno. Tangoganiza, tsiku lina ndinadzuka, kusukusula n’kupita kwa Mtsamunda Williams. Ndinamuuza kuti: ‘Ndinu mtundu wa anthu okhala ngati nthata, mumakhala pakati pathu n’kumatiyamwanso magazi. Dziwani kuti ngakhale kunja kutakhala mdima wotani, kunja kumacha basi! Ndipo masiku onse samacha mofanana. Lero ndi tsiku lina ndipo dzu- wa likuwala bwino m’mlengalenga. Taleka ndikufunse mafunso angapo: Kodi ndi ndani amene anamanga nyumba imeneyi? Ndindani amene anaswa mphanje m’mindayi? Ndiye tsopano ndimvetsere mosamala. Womanga akufuna umubwezere nyum- ba yake ndipo wolima akufuna minda yake. Kodi munthu wokolola pamene sanafese akuganiza kuti iyeyo ndi ndani? Ko- di akuganiza kuti iyeyo ndiye woimira Mulungu padziko lapansi pano? Zipita komwe unachokera, chifukwa kuyambira lero, omanga sakufunanso kuti azichita kupempha malo oti agone; olima sakufunanso kuti azigona ndi njala; atelala sa- kufunanso kuyenda osavala; munthu yemwe amagwira ntchito sakufunanso kusiyira njenjete chuma chomwe amachikhetsera thukuta. Ndinaimba kuti: 75