Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 78

Matigari nthawi yomweyo anagwera pansi. Aliyense amene ankaonerera macheza a anthu awiriwa, sankayembekezera kuti zimenezo zin- gachitike. Ngakhale Guthera ndi Muriuki anadabwa kwambiri pamene ankaona nkwapulo ukuuluka m’malere n’kutera pathupi la Matigari mochita phokoso lalikulu. Pamene munthu wakudayo ankakwezanso chikwapu chija kuti amulembe nachonso kachitatu, mzungu uja analowererapo. “Ugwereni mtima achimwene, chachitika n’chiyani?” anafunsa adakali pahatchi pomwe paja. “Eti munthuyu akunyoza bambo anga . . . ine ndikumva. Ndi wopanda khalidwe! Ofunika kumuphunzitsa mwambo.” “Wanenanso kuti akuwadziwa? Kodi mesa bambo ako anasowera limodzi ndi bambo anga?” “Inde, chitsiruchi chikuoneka kuti chikudziwa zambiri. Ndichium- budza mpaka chitafotokoza bwinobwino zonse.” “Mtima pansi. Osaiwala kuti mukungopanga sewero. Mbali yovu- ta ya seweroli inaseweredwa kale ndi makolo athu. Ukhoza kumufun- sanso mafunso ena angapo. Mwina angatithandize kudziwa chimene chinawachitikira.” Matigari anapititsa manja ake m’chiuno mwake. Koma ana- kumbukira kuti wadzimanga ndi lamba wamtendere. Monga munthu wamwamuna, anayesetsa kupirira kuti asaonetsere pagulu kuti akumva ululu woopsa ndipo anadzuka pamene anagwera paja mwapang’onopang’ono ngati nkhalamba yodwala nyamakazi. Kenako anagwira geti lija kuti limuchiri- kize ngati ndodo yake. Dzuwa linali litabira tsopano, komabe linasiya kamtambo kofiira ngati magazi komwe kankawalabe madzulowo. Kamtamboko kankachititsa kuti nyumba ija, pageti komanso nsewu womwe anthu aja anaima ziziwala. 77