Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 43

Matigari Gawo 8 Pakhoma pa balayo panajambulidwa chithunzi cha nyama zakuthengo. Panali njovu, fisi, njati, njoka, kambuku komanso mbidzi zitakhala mozungulira. Nyama zonsezi zinali zitanyamula botolo la mowa m’manja mwawo. Mfumu Mkango ndi imene inakhala pakati pawo, ndipo inkatolera ndalama. Pachisoti chake chachifumu, panalembedwa kuti “Mfumu ya M’nkhalango.” Pamimba pake panalembedwa kuti, “msonkho,” ndipo pafupi ndi miyendo yake panali m’golo wamowa. Pamgolowo panalembedwa kuti, “Papirani, Papirani. Imwani Zenizeni! Ndiponsotu Mowa Ndi Wotchipa. ” Mayi wina wonenepa anakhala pamalo ogulitsira zakumwa ndipo pamalowa panali potetezedwa ndi zitsulo. Pafupi ndi mayiyu, panalinso mayi wina wonenepanso ngati yemweyu ndipo onse anavala madiresi oyera. Azimayiwa ankakambirana nkhani ya kunyanyala ntchito inali m’kamwam’kamwa ija. “Ndiye tizitani akatseka fakitaleyi?” Mawu awo ankamvekera pansipansi chifukwa mtibu wa mubalamo unakwezedwa kwambiri ndipo pa nthawiyi n’kuti pakuseweredwa nyimbo yakuti “Shauri Yako*.” *Shauri Yako (Kiswahili): Kutanthuza: kuti “Limenelo ndi vuto lako, zako zimenezo.” Matigari ndi Muriuki anakhala patebulo lapakona chakumapeto kwanikweni kwa balayo. Matigari anakoleka chipewa komanso chijasi chake chija pampando. Mayi mmodzi anatuluka kogulitsira kunja n’kudzawafunsa kuti akonda kudya chiyani. “Kodi masiku ano azimayi amagwiranso ntchito kubala?” Matigari anafunsa Muriuki. “Azimayitu amagwira ntchito paliponse,” anayankha motero 42