Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 44

Matigari Muriuki. “Amasesa kufakitale, amapalira m’minda, amathyola tiyi ndi khofi, amafukula mapaipi otsekeka komanso amakonza ngalande zodutsa madzi onunkha.” “Nanga mayi ako? Mayi ako amagwira ntchito yanji?” “Mayi anga? Mayi angatu anamwalira.” “Ulibe bambo komanso mayi? Ndiye kuti ndiwe mwana wamasiye? Chinawachitikira n’chiyani mayi akowo? Ankadwala?” “Munthu wina anayatsa nyumba yathu ndipo mayi anga anapsera momwemo.” “Munthu wina anayatsa nyumba? Anayatsayo ndi ndani?” “Alandilodi athu. Mayi anga ankapanga lendi nyumba ya munthu wina koma ankalephera kulipira. Ndiye tsiku lina alandilodi anawauza kuti atulukemo m’nyumbamo, koma mayi anga anakana. Anawauza kuti: ‘Mukuganiza kuti ndilowera kuti mukandithamangitsa m’nyumbayi? Simunganditulutse m’nyumbamu n’kundisiya patchire ngati nyama. Zoona mulibe chisoni! Mukufuna kuti ndife? Kodi ndalama ndi moyo wa munthu chofunika kwambiri n’chiyani?’ Ndiyendo alandilodiwo anati: ‘Mutuluke m’nyumba yangayi! Muona kolowera, ine ndiye ndizikakudyerani kuchipatala? Mutulukemo m’nyumbamu kaya mukufuna kapena ayi. Muchoke pano tatopa nanu!’ Madzulo a tsikulo, mayi anabwera kunyumba ataledzera ndipo anangofikira kugona. Chapakati pa usiku, ndinadzidzimuka nditamva fungo la utsi. Ndinathamangira kumene amayi anagona koma ndinawapeza atatapatikiratu ndi tulo. Ndinayesetsa kuwagunyuza, ndipo anadzukadi. Ananditulutsa panja kudzera pazenera. Koma iwowo sanakwanepo chifukwa zeneralo linali laling’ono. Ndiyeno 43