Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 30

Matigari padzakhala mtendere ngati kumwamba. N’kutheka kuti sanamve pamene mwana uja ankamuchenjeza kuti asalowe m’mudziwo. Iye anayendabe ngati njovu kulowa m’mudzi wa ana uja. Kenako anangozindikira mwala wamudutsa. Mwamwayi unamuphonya chifukwa ukanamupeza ukanamuchotsa diso. Posakhalitsa winanso unatera pafupi ndi mwendo wake. Anangozindikira winanso ukubwera ngati wapalegeni moti akanapanda kuzinda ukanamuswa. Apa mpamene anazindikira kuti anawo amagenda iyeyo. Mwana ankamenya mnzake uja anali ataima pamwamba pa Mercedes-Benz, akuitana anzake n’kumawauza kuti m’mudzi mwawo mwalowa m’maliwongo yemwe akufuna kuwabera zinthu zimene atola. Kenako bambo uja anaima kwi! Pa nthawiyi n’kuti miyala ija ikuvumbwa kuchokera mbali zonse. Kenako anapalapasa m’chiuno mwake pamene ankaika pistole yake ija, koma anakumbukira kuti wavala lamba wamtendere. Komanso anazindikira kuti anali ana chabe, sanali ngati mdani analimbana naye kwa zilumika zambirimbiri uja. Modabwa ndi zimene zinkachitikazo, anaima njo n’kunena kuti, “Ana anga!” Mwana anali naye uja anazindikira kuti paipa. Anathamanga n’kukamugwira bamboyo mkono n’kuyamba kutuluka naye m’mudzi muja. Bamboyo anayamba kutsatira mwanayo asakumvetsa kuti chikuchitika n’chiyani. Ana ena aja ataona kuti akuthawa, anayamba kukuwa kwinaku akuvunga miyala mwamphamvu n’kumamuperekeza nayo bamboyo pamene ankathawa molowera kumene kunali chipata cha fakitale ija. Pa nthawiyi n’kuti nkhope yake itagwa chifukwa cha chisoni ndi zimene 29