Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 31

Matigari zinkachitikazo. Tsinya linali pholipholi pachipumi. Zinkaoneka kuti anali ndi mwayi kwambiri chifukwa miyalayo inkangomuphonya. Palibe mwala womwe unamufika m’nthupi. Galimoto zonyamula mabwana a ku Ulaya, ku Asia komanso ku Africa zinkangoti vuu, vuu! Ena anaimitsa galimoto zawo kuti apereke mpata kwa oyenda pansi kuti awoloke kwinaku akusangalala kuonerera gulu la ana lija litapanikiza munthu wachikulire ndi miyala. Ena ankangoonerera ali m’magalimoto awo sewero lomwe linkachitikalo. Ena anali atatsamira galimoto zawo, kwinaku akupyontha Co ca-cola ndipo ena ndudu zinali zili pakamwa, utsi uli phaa! Panalinso ena ambiri omwe ankaonerera zimene zinkachitikazi. Eniake a maokala komanso ogula malonda anaima m’makomo komanso panja ali m’magulu n’kumaonerera munthu wamkulu atapezeketsedwa ndi miyala. “N’chifukwa chiyani anawa akugenda wamisalayo?” ena anafunsa. Ena ankangopukusa mitu n’kunena kuti, “Ana ndi amisala amadana kwambiri. Amangokhala ngati mphaka ndi khoswe.” Bambo uja sanasinthe mmene ankayendera komanso ankaoneka kuti sakuzindikira kuti ali pangozi yaikulu. Anachotsa chijasi chake chija kuchoka paphunzi lina n’kuchiika paphuzi lina. Pamenepo n’kuti pachipata cholowera kufakitale kuja pakutuluka unyinji wa ogwira ntchito omwe ankapita kukadya nkhomaliro. Mwana uja anamusiya bambo uja n’kuthawira kuchipata kuja. Bamboyo anatsala yekha pakatikati pa anthu oonerera, ogwira ntchito kufakitale aja komanso ana ankamugenda aja. Pa nthawiyo kunja kunkatentha ngati muuvuni. 30