Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 3

Matigari mwini nyumbayo n’kukhala pakhonde, alendowa anatenga ma- lo onse abwinoabwino. Anatenganso chilichonse chaphindu kuphatikizapo mphamvu za eni malowo. N’kupita kwa nthawi chifukwa cha kulimba mtima kwa anthu omenyera ufulu wadziko lawo, anakakamizika kupereka ufulu, koma anapitirizabe kulamulira pogwiritsa ntchito anthu ena akuda omwe anawaika pamipando ndipo nawonso anayamba kupondereza anzawo aja ndi nkhan- za zosaneneka. Buku la Matigari limasonyeza nkhondo zomwe zinachitika pakati pa anthu omenyera ufulu wawo ndi olamulira achit- samunda omwe ankafuna kumanga maganizo a anthu akuda mu ukapolo. Koma ena ozindikira komanso olimba mtima anai- ma nazo n’kuyamba kunena kuti zinthu zomwe anazikhetsera thukuta zibwerere kwa eni ake. Anthuwa anayamba kukana kuti atsamunda komanso antchito awo azikolola pamene sanalime. Limasonyezanso zimene boma linkachita kuti m’malo mothan- diza anthu linkakonda kuchita zinthu zoti mayiko ena alitame. Komabe sindigwirizana kwenikweni ndi zimene Ngugi ana- sonyeza m’bukuli kuti choonadi ndi chilungamo chingapezeke kokha ngati anthu atagwiritsa ntchito mphamvu polimbana ndi amene akuwaponderezawo, mwinanso kufika pokhala okonze- ka kufa pomenyera ufulu wawo. Ine ndimaona kuti zimenezi zimangokolezera mavuto. Mfundo yosatsutsika imene ndimaona ndi yoti anthu sangakwanitse kulamulirana okhaokha zinthu n’kumayenda popanda vuto lililonse. Chifukwa cha ku- chuluka kwa anthu adyera m’dzikoli, anthu ambiri amapwetekeka chifukwa cha zochita za anthu ochepa odzikon- da. Ngugi anapereka chithunzi chabwino cha zimene zimachi- tika anthu akakhala ndi mtima wa kokerakwako. 2