Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 2

Matigari Mawu Oyamba Buku la Matigari linalembedwa ndi Ngugi wa Thiong’o ndipo linasindikizidwa koyamba ndi kampani ya Heinmann mu 1989. Bukuli linamasuliridwa m’Chichewa chothyakuka ndi Bonwell Rodgers. Mwachidule, bukuli limafotokokoza za msilikali wina wagulu la Mau Mau yemwe anabwerera kwawo atakwirira zida zake n’kuvala “lamba wamtendere.” Iye ankafu- nitsitsa kukasonkhanitsanso anthu a mtundu wake komanso kuyamba moyo watsopano. Koma m’malo mwake anakapeza dziko litazondoka, zinthu zisakuyenda mmene ankaganizira. Kuti akonze zinthu, anayamba kufunafuna choonadi ndi chi- lungamo. Iye anazungulira m’dziko lonse koma sanapeze pame- ne pankachitika chilungamo ndipo anapeza kuti anthu ake ankangolimidwa pamsana ndi atsogoleri achinyengo omwe ankangofuna kukhutitsa mimba zawo. Pamapeto pake anapeza kuti ntchito yake yofunafuna choonadi ndi chilungamo inangopita padera. M’bukuli Ngugi anasonyeza kuti anthu akhoza kupitirizabe kuponderezedwa ndi olamulira awo ngati patapanda kupezeka munthu wolimba mtima woti ayankhule komanso amenye nkhondo n’kuthetsa kupanda chilungamoko. Bukuli limafutukula mmene atsamunda anakokotera chuma cha ku Africa kuno n’kuwasiya eni dziko akuzunzika koopsa ndi umphawi. Limasonyeza kuti alendowa anabwera kudzapempha malo, koma ankasangalala kuposa eni dziko. Kenako anayamba kulanda malo ndi zinthu zina moti anasiya eni malowo manja ali m’khosi. Mofanana ndi njovu yomwe inapempha muthu wina malo oti ibisale mvula, n’kupezeka kuti yadzadza m’nyumbamo 1