Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 258
Matigari
Iwo anazindikira kuti apolisi akumutsata ndipo chidwi
chawo chinali pagalimoto za apolisi zomwe zinkayenda
pang'onopang'ono m'mbuyo mwa Matigari zija. Iwo sankadziwa
kuti chamuchitikira n'chiyani kuti azilondoledwa ndi apolisiwo
komanso kuti akanatani kuti adzipulumutse. Iye anali atazungu-
liridwa ndi adani.
Apolisi omwe anaima pageti lolowera kumpanda wanyumba
ija anatsegula geti ndipo anachita saluti n'kulola kuti Matigari
alowe kumpandako. Iwo sankadziwa kuti akulowetsa chilombo.
Ankangodzifunsa kuti: ‘Kodi nduna imene yabwerayi ndiye iti?’
Aliyense ankadzifunsa funso lomweli. ‘Kodi kumbuyo kwa Mer-
cedes-Benz'yo kunali nduna iti?’ Komabe sankadabwa
kwenikweni ndi kubwera kwa ndunayo kuchochitikachi. Iwo
ankadziwa bwino mmene m'mimba kwa akuluakulu a boma ko-
manso achipani cholamula munkabwadamukira akaganizira za
kubweranso kwa Matigari ma Njiruungi. Iwo ankaganiza kuti,
‘Ngakhale Matigari atakhala kuti ndi Khristu, ayenera kuman-
gidwa mwansanga kapena kuwomberedwa akabwera ku-
malowa.’
Matigari anayendetsa galimoto ija n'kumalowera chakugala-
ja, ndipo mofulumira anaponda buleki ndipo galimotoyo ina-
khwekhwereka n’kutembenuka, moti mphuno yake inaloza ku-
mene kunali geti kuja. Kenako anaiyendetsa mpaka pamene
panali khomo lolowera m'nyumba ija.
Galimoto za apolisi zinkayenda pang'onopang'ono zija zinai-
ma mwadzidzidzi panja paja. Apolisi omwe anali m'galimotozo
anatuluka mofulumira mifuti ili m'manja. Giceru, kazitape uja
anatulukanso nawo limodzi. Wina ananyamula kawailesi meseji
m'manja ndipo anayamba kuyankhula.
257