Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 25

Matigari “Azibambo enaake, anthu ngati inuyo,” mwanayo anayankha motero. Kenako anamezera mate n’kunena kuti, “Koma akayerekezanso kuchita zimenezi aona mbwadza.” “Bwanji?” “Taphunzira njira zodzitetezera. Tikumawagenda ndi miyala, apo ayi tikumagwira m’modzi ndikumuphwanya.” “N’chifukwa chiyani mumalipira kuti mulowe kumtaya kuja? Kodi mumakhala mukulipira msonkho kapena?” “Ayi. Azibambo awiri munawaona aja anangoyamba kumaima pageti paja n’kumatiuza kuti tiziwalipira.” “Chimachitika n’chiyani ngati simunalipire?” “Ee! Amatikhudula! Tsiku lina anatiwaza mambama.” “N’chifukwa chiyani simunangogwirizana kuti muwatibule kapena kuwagenda ngati mmene wanenera muja? Mwinanso munakangopita kupolisi n’kukawanenera.” “Kupolisi? Mulitu ndi chibwana inu! Apolisi ake ati? Poti apolisi ndi mbava zimenezi amadziwana. Anthu amenewa amangoti khethekhethe ngati zala za dzanja langali,” anatero mwana uja akumusonyeza bambo uja dzanja lake. “Tikangopanda kupereka, apolisi amayamba kutisakasaka n’kumanena kuti taba zinthu, kapena kutiletsa kulowa kumtaya kuja ponena kuti tikatengako kolera n’kupatsira anthu ena. Nthawi zina amatithamangitsa m’nyumba zathu n’kumanena kuti ndife amasikini.” “Umakhala kuti?” “Kunyumba yanga.” “Nyumba yako? Ili kuti?” “Mukufuna mukaione?” 24