Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 197

Matigari "Anduna!" Matigari anaitokosa motero nkhani. "Pajatu ndi- nakufunsani funso koma simunandiyankhe. Mwina ndichite molibwerezanso. Kodi ndi kuti m'dziko lino kumene munthu amene wadzimanga ndi lamba wamtendere angapeze choonadi ndi chilungamo?" Nduna ija inachita chibwibwi. Inkaoneka kuti sinakonzeke kuti Matigari aifunsaso funsolo. Kenako inatembenukira kwa anthu anali muholomo. "Munthu ameneyu yemwe akumadzitchula kuti ndi Matiga- ri ma Njiruungi akuyenera kunyongedwa. Kodi simunamve pamene amavomereza yekha kuti anapha anthu? Koma oweru- za athu amupeza kuti ndi wopenga. Wofufuza milandu wovala chipewa choonetsa maso okha uja anavomereza kuti Matigari anagawira anzake onse omwe anamangidwa nawo, buledi komanso mowa potengera zimene Yesu anachita pa Mgonero wa Ambuye. Nokhanso munamumva apa akubwebwetuka kuti wakhala m'nkhalango komanso m'mapiri kwa zaka zambiri akumenyana ndi Boy komanso Williams. Zonsezi zikungosonyezeratu kuti munthuyudi ndi wozerezeka. Major Howard Williams ndi John Boy anapita kukamenyana ndi zigawenga pa nthawi yomwe nkhondo yomenyera ufulu inkachitika, mwina titero kunena kwake kuti mumvetse. Zimamveka kuti anafa pamene ankamenyana ndi zigawengazo. Anthu awiri amenewa anapatsidwa mamendulo aulemu chifukwa cha kulimba mtima kwawo komanso mtima wawo wololera kufera ena: A Williams anapatsidwa CBE (Commander of the British Empire), ndipo Boy anapatsidwa MBE (Member of the Order of the British Empire). Komano taganizani, kodi mukuganiza kuti munthu amene mutu wake ukugwira ntchito bwinobwino angabwere pagulu pano 196