Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 196

Matigari amenewa ndi amene amayambitsa mpungwepungwe komanso magawano m'dziko muno. Ndi anthu ngati omwewa amene akuchititsa kuti asilikali ayambe kugalukira boma. Funso limene anafunsa lija likusonyeza kuti mawaya ena a m'mutu mwake anaduka, mutu wake sukoka. Choncho oweruza athu agamula kuti apititsidwe kuchipatala cha anthu amisala kuti akaone nga- ti mutu wake ukuyenda bwinobwino . . . Ndiye mwaonatu, og- wira ntchitonu mumatsogoleredwa ndi munthu waziwala m'maso." Asanatulutsidwe panja, Ngaruro wa Kiriro anakuwa kuti: "Mukhoza kundimanga ineyo, koma dziwani kuti ogwira ntchi- to sadzaleka kumenyera nkhondo ufulu wawo!" Poyankha nduna ija inati: "Mwaona mmene maganizo opotoka angasocheretsere munthu!" Kenako nduna ija inatembenukira kwa Matigari ma Njiruun- gi. Matigari anali ataima nji ngati chitsa chotsala mulupsa ndipo ankangooneka ngati chiphona. Iye sankatekeseka mpang'ono pomwe. Ndi khalidwe limeneli limene linkachititsa kuti anthu azimuopa. Ankayang'ana ndi diso lachiweruzo, diso lokhala ngati mpeni. Ndipo akamayang'ana munthu ankakhala ngati akumuona ndi matumbo omwe. Nduna ija sinkayang'anana ndi Matigari maso ndi maso. Kenako inayamba kuchita zinthu mokayikakayika ndipo zinayamba kukhalanso ngati yataya lilime lake moti pamene inali mkati molifunafuna, Matigari ana- pezerapo mpata woyankhula. Tsopano zinkangokhala ngati asinthana mbali. Iyeyo anayamba kuchita zinthu ngati ndi amene ali Nduna Yoona Zachilungamo ndipo ndunayo inkakhala ngati ikuuzidwa chi- gamulo. 195