Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 198

Matigari n'kumadzitama kuti anapha anthu? Ndiponso mafunso amene akufunsawa, kodi angatuluke pakamwa pa anthu omwe pakati pa mapewa awo pali mitu yabwinobwino ngati wa ine komanso yanuyo? Oweruza athu aona kuti mutu wa munthu ameneyu ndi wosukusa ndipo akuyenera kupititsidwa kuchipatala cha anthu amisala. Akapita kumeneko akaikidwa pamalo achitetezo chokhwima kwambiri, chifukwa ndi munthu woopsa komanso ali ndi maganizo aupandu m'mutu mwakemu." Kenako Matigari anatembenuka mwadzidzidzi moyang'ana Nduna Yoona Zachilungamo ija, mkulu wa apolisi, oweruza aja, bwanamkubwa uja, wansembe, Boy, Williams, pulofesa wokha- zikika wa Parro to lo gy komanso alendo ena onse olemekezeka omwe anali kutsogolo kuja. Iye anayamba kuonekanso wachinyamata ndipo mawu ake anayamba kumveka ngati chiphaliwali. "Nyumba ija ndi yanga chifukwa ndinaimanga ndi manja anga. Mindanso ndi yanga chifukwa ndine ndinailima. Mafakitalenso ndi anga chifukwa ndinawamanga komanso ndinkagwirako ntchito. Sindidzasiya kumenya nkhondo kuti mundibwezere zinthu zimenezi. Ndinakhetsa magazi popanga zinthu zimenezi ndipo sindingawakhetse pachabe. Tsiku lina minda idzabwerera kwa mwini wake mlimi, komanso chuma cha m'dzikoli chidzabwerera kwa amene amachipanga. Umphawi komanso mavuto ayenera kudzathetsedwa m'dziko lathu lino!" Kenako Matigari analoza Robert Williams ndi John Boy ngati mmene amachitira munthu amene akukalipira mwana. "Ndiponso iweyo munthu wankhanza komanso wantchito wakoyo, ndiponso zidole zanu zonsezi, izi zili kutsogolo kuno, ndikunena ndunayi, akuluakulu a apolisi, akuluakulu a asilikali, 197