Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 19

Matigari komwe kuli ana ake komanso anthu a mtundu wake. Maganizo akewa anadodometsedwa ndi phokoso la ana ena. Atatembenuka anaona gulu la ana akuthamanga pakati pamsewu. Anadzifunsa kuti, “Kodi akuthamangira chiyani?” Kenako anaona chigalimoto chofiira chija chikutuluka mumsika muja. Ngolo zake zinali zitadzadza kwambiri ndi zinyalala zina zomwe inakatenga mumsika muja. Anadzifunsanso kuti, “Koma nanga n’chifukwa chiyani anawa akuthawa chigalimotocho? Ana angaaa!” Sanayankhulenso ndi mlonda uja. Iye anayenda mofulumira kutsatira ana komanso chigalimoto chija. Mtima wake unkagunda mofulumira. Iye ankadziuza kuti, “Odi ndifulumire kuti ndikawauze kuti ndabwera ine bambo awo. Ndikawauze kuti moyo wothawathawa tsopano watha, ndikufuna kubwerera kunyumba. Tonse tipite kunyumba kwathu. Tikalomwe m’nyumba mwathu limodzi. Tikakoleze moto limodzi. Ndipo pajatu nkhani yomwe inachititsa kuti tilimbane ndi atsamunda inali yokhudza nyumbayi, si choncho paja? Tinkafuna nyumba yathu, malo achitetezo, kuti ana athu azidzasewera pakhonde komanso azidzapanga ndado pabwalo. Tizidzagawana zochepa zimene tili nazo. Tizidzasangalala pambuyo pokumana ndi zokhoma, kuzizidwa, kukhaula ndi njala, kuyenda chinochino chifukwa cha usiwa, kusowa tulo, kutopa komanso kupulumuka lokumbakumba. Kuti ugonjetse adani ako umafunika kulimba mtima. Usiku ungatalike bwanji, kunja kumacha basi.” Iye sanakhulupirire zimene anaonazi. Anadzifunsa kuti, “Kodi zimenezi zikuchitikanso masiku ano, m’dziko laufulu ngati limeneli? Koma zoona zimenezi zikuchitika dzuwa likuswa mtengo?” 18