Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 57

Sewero la Mfumu Edipa KUZUKUTA MWACHIDULE ZOCHITIKA M’SEWEROLI Zaka khumi ndi ziwiri zochitika za m’seweroli zisanachitike, Edipa ana longedwa kukhala mfumu ya ku Thebesi atachita zakupsa populumutsa anthu a mumzindawu kuchokera kwa chilombo china chomwe chinayi- ma pachipata cholowera mumzindawu. Chilombochi chinkadya anthu moti palibe ankalowa kapena kutuluka mumzindawu. Chilombochi chinathawa pamalowa n’kukadzipha Edipa atayankha molondola ndagi yomwe chilombocho chinkapereka. Ndiye popeza mfumu Layasi yo- mwe inkalamulira Thebesi inali itangophedwa kumene, anthu analonga Edipa kukhala mfumu yawo chifukwa chowapulumutsa. Anamupatsa- nso Yokasi, yemwe anali mkazi wa mfumuyo kuti akhale mkazi wake. Ndiye tsopano, mliri winanso wowopsa kwambiri unabuka ku Thebesi ndipo anthu anapita kwa Edipa kukamupempha kuti awapulu- mutsenso ku mliriwo ngati mmene anachitira ulendo wapita. Mfumuyo inkawoneka kuti yamvetsa vuto lawo. Ndiyeno Kireyo, mchimwene wa mkazi wake Yokasi, anatulukira kuchokera ku Defi komwe anakafunsira kwa mulungu wina dzina lake Apolo. Mulunguyo anawawuza kuti zinthu zikhoza kuyambanso kuyenda bwino ngati munthu amene ana- pha Mfumu Layasi atathamangitsidwa mumzindawo. Poyesayesa kupeza anthu amene anapha mfumuyo, Edipa anayita- nitsa wolosera wina dzina lake, Teresi. Teresi anakana kuwuza mfumu- yo zimene anawona, koma mfumuyo inayamba kumuwumiriza kuti anene chilungamo chokhachokha ndipo iye anawuza Edipa kuti iyeyo ndi amene anapha Mfumu Layasi. Edipa anakwiya kwambiri ndi mawu amenewa moti anayamba kuyimba mlandu Kireyo, mlamu wake uja, kuti ndi amene wagwirizana ndi Teresi kuti adzanene bodza n’cholinga choti alande ufumu. Pa nthawiyi mpamene Yokasi anatulukira ndipo anawuza mwamuna wakeyo kuti olosera ndi anthu achinyengo koma- nso osathandiza. Pofuna kumutsimikizira mfundo imeneyi, anamufoto- kozera za ulosi wina womwe unkanena kuti mwana yemwe Yokasiyo adzabereke adzapha bambo ake n’kukwatira ndi mayi ake. Pofuna ku- mutambasulira bodza lokhudza ulosiwo, anawuza Edipa kuti mwa nayo anaphedwa n’kukatayidwa kumapiri komanso kuti mwamuna wake Layasi anaphedwa ndi achifwamba patapita zaka zambiri, pamalo ena 52