Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 96

Paphata pa Chichewa Khuta mavuto: Kutopa ndi mavuto. Chitsanzo: Anthu ambiri amene amadzikhweza amakhala oti akhuta mavuto. Khutaufe: Kudya zomwe zatsala kuti kenako ufe. Chitsanzo: Chakudya chomwe tatsala nacho ndi khutaufe. Khutchakhutcha: (a) Mawuwa amanenedwa ngati munthu wonenepa kapena wamkulu akuvina kapena kuyenda movutikira. Chitsanzo: (1) Ndinakumana nawo ali khutchakhutcha. (2) Povina amachita kuti khutchakhutcha. Khutu limodzi: Kumva pang’ono. Chitsanzo: Nkhaniyo ndinaimva ndi khutu limodzi. Khutula phutula: Kuyesetsa kuyenda uku ndi uku kuti upeze thandizo. Chitsanzo: Atazingwa, amangoti khutula phukula, kusakasaka woti awathandize. Khuzumuka: Mawu amene anthu amanena pouza munthu wina kuti adekhe, asapupulume. Chitsanzo: Chonde achimwene khuzumukani. Khwangwala: Munthu wamantha. Chitsanzo: Inutu ndi khwangwala, kumangochita mantha ndi chilichonse! Khwasukhwasu: (s) Kuyenda osatenga kanthu kumanja. Chitsanzo: Amangoyenda khwasukhwasu pobwera kuno. (b) Ndiwo zanyama. Chitsanzo: Madzulo ano tidyera khwasukhwasu. 95