Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 95

Paphata pa Chichewa Khope: Kuchita mwayi kapena kuuzidwa kuti uchite zomwe umafuna kale. Khope ndi mbalame imene imakonda kuulukira kumene kukupita mphepo. Mawuwa amagwira ntchito ponena za munthu amene watumidwa chinachake, iyenso ali ndi zochita zina komweko, moti popita sanyinyirika. Chitsanzo: Ndimadabwa kuti anasangalala kwambiri nditamutuma kupita kumeneku. Sindimadziwa kuti ndikutumiza khope. Khuluku: Mawu obwerekera kuchingerezi onena za mun- thu wosadalirika komanso wopanda pake. Chitsanzo: Bamboyu ndi khuluku. Khumata: Khala mwamantha. Chitsanzo: Ukufuna anawa azikhala mokhumata chifukwa cha iwe! Khumbi: Kanyumba komwe anthu amamanga kumunda kuti azindikirira apusi kapena nyama zina zomwe zinga- wadyere mbewu zawo. Amagwiritsanso ntchito kanyumba- ka popuma akatopa ndi kulimba ndiponso amasungamo zinthu zina. Chitsanzo: Mukamaliza mundipeza kukhumbi. Khumbira: Kusirira, kufuna chinachake kwambiri. Chitsanzo: Mtsikana uja ndimamukhumbira. Khumucha: Munthu wolemera. Chitsanzo: M’dala amene uja ndi khumucha. Khumudwa: Kusakondwa. Chitsanzo: Ataona kuti nsima yake yadyedwa, anakhumudwa kwambiri. 94