Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 55

Paphata pa Chichewa padzaphuka kanthu. Dzala: (a) Munthu wodya kwambiri komanso mosasankha. Chitsanzo: Pakamwa pawo ndi padzala. (b) Munthu yemwe amangomupatsa zinthu zakutha. Chitsanzo: Ifetu ndiye ndi dzala, amatipatsa chinthu chikatha. Dzandidzandi: Kuyenda mosakhazikika ngati ukufuna kugwa. Nthawi zina munthu amayenda chonchi ngati waledzera. Chitsanzo: (1) Atasenza thumbalo anayamba kuyenda mwadzandidzandi. (2) Ndinakumana nawo ali dzandidzandi. Dzanja lasefa: Dzanja losasunga ndalama. Chitsanzo: M’tauni muno ukhoza kutuwa koopsa ngati utakhala ndi dzanja la sefa. Dzanja limodzi: Ndekha, yekha, okha. Chitsanzo: (1) Ukamalima munda waukulu umafunika kukhala ndi aganyu, osati dzanja limodzi. (2) Dzanja limodzi lingakwanitse bwanji kuchita zonsezi? Dzaoneni: Chinthu ngati chafika poipa kapena chakula kwambiri timati chafika padzaoneni. Angatanthauzenso zinthu zochuluka. Chitsanzo: (1) Ali ndi ndalama zadzaoneni. (2) Ali pa umphawi wadzaoneni. Dzera kunkhongo: Kusadziwa zinazake, kusazindikira kodabwa. Chitsanzo: Ndinenapo bwanji maganizo anga popeza 54