Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 376

Paphata pa Chichewa (2) Amuwamba ndi chitsulo chamoto. (b) Chinthu chofala, chinthu chomwe si chapamwamba, munthu yemwe alibe udindo ulionse, munthu wosauka. Chitsanzo: (1) Kuno sikulowa anthu wamba. (2) Sindingagule njinga za wamba. Wamfupimapazi: Mkazi. Chitsanzo: Wachita zimenezi ayenera ndi wamfupimapazi. Wamtalizala: Munthu wakuba. Chitsanzo: Chenjerani naye munthuyu, ndi wamtalizala. Wamutu wofuna jeke: Wamkulu mutu. Chitsanzo: Ndani anakuuza kuti anthu amitu yofuna jeke amakhala anzeru? Wamutu woipa: Munthu yemwe amalota maloto oipa kwambiri. Chitsanzo: Ndikaona zinthu zochititsa mantha sindigona. Mutu wanga ndi woipa. Wamutu wophikika: Wosokonekera, wopanda nzeru. Chitsanzo: Ana awo ndi a mitu yophikika. Wamutu wosukusa: Wopanda nzeru. Chitsanzo: Asabwere kuno amene uja, sitifuna anthu a mitu yosukusa. Wamvulazakale: Munthu wakalamba. Chitsanzo: Amvulazakale akumaganiziridwa kuti ndi afiti. Wamwera zake: Waledzera kwambiri. Chitsanzo: Ndakumana naye ali dzandidzandi. Zikuoneka kuti wamwera zake. Wandikama: Wandidyera ndalama zanga zonse, akungofuna ndimupatse ndalama. Chitsanzo: Akabwera pakhomo pano n’kufunsa dzina langa, ndimachita kudziwiratu kuti akufuna andikame. Wanditengamo: Wandipsetsa mtima. Chitsanzo: Mnyamata amene uja wanditengamo. Zoona kufupika kumene kuja angandiuze kuti amandifuna? 375