Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 373

Paphata pa Chichewa Wachiyera: Nzungu. Chitsanzo: Kukubwera munthu wachiyera. Wada (wachita mdima): Wachita manyazi. Chitsanzo: (1) Nkhope yake yachita mdima. (2) Mnyamata uja wada. Waduka lende: Kukumana ndi mavuto. Munthu ukakhala palende lendeyo n’kuduka umagwa pansi. Chitsanzo: Mkaziyu azunzika koopsa chifukwa anaduka lende, mwamuna wake atangomwalira. Wadya ndalama: Wawononga ndalama. Chitsanzo: Munthu ameneyu wadya ndalama zanga. Wadyapo: Mawu amene anthu amanena mwachipongwe wina akapweteka. Mawuwa amatanthauza wachita bwino wapweteka. Chitsanzo: “Ndinakuuza kuti uziyang’ana pansi. Wadyapo!” Wadyera pamwamba: Wadziwika. Chitsanzo: Amayenda m’mbali, lerotu wadziwika. Amugwira akudyera pamwamba. Wadyera zake (wamwera zake): Waledzera kwambiri. Chitsanzo: Ndakumana naye ali dzandidzandi. Zikuoneka kuti wadyera zake. Wadzitho: Wamphamvu. Chitsanzo: (1) Akufuna anyamata adzitho. (2) Mnyamatayu ndi wadzitho. Wafawafa: Kulimbana kwambiri pampikisano. Chitsanzo: Masewerawa afika mundime ya wafawafa. Wafodya: Wopanda nzeru. Chitsanzo: Akulu amene aja ndi afodya, asadzabwerenso kuno! 372