Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 372

Paphata pa Chichewa Wa Adamu: Kuyenda wapansi. Chitsanzo: Ngakhale sukulu yawo ili kutali, mnyamatayo amayenda wa Adamu. Wachabe: (a) Munthu woipa. Chitsanzo: Munthu amene uja ndi wachabe. (b) Katswiri. Chitsanzo: Mwanayu ndi wachabe pankhani ya mpira. (c) Kubwera opanda kanthu. Chitsanzo: Angoyenda wachabe. Wachabechabe (chachabechabe): Wopanda ntchito, wosafunika, chinthu chakutha. Chitsanzo: (1) Wantchitoyu ndi wachabechabe. (2) Andigulitsa wailesi yachabechabe. Wachamba: (a) Wopanda nzeru. Chitsanzo: Ndiwe Wachamba eti? (b) Munthu amene amasuta chamba. Chitsanzo: Panadutsa bambo wachamba uja. Wachepa: Ndi mwana. Chitsanzo: Wachepa, sungalimbane ndi ine. Wachikulire: (a) Munthu wokalamba. Chitsanzo: Bambo awo ndi achikulire. (b) Bwana, wolemekezeka. Chitsanzo: (1) Amene uja ndi wachikulire pakampanipa. (2) Ameneyu ndi wachikulire pa nkhani zoimbaimbazi. Wachimasomaso: Munthu wokonda amuna kapena akazi, hule. Chitsanzo: (1) M’nyumba iyi mumakhala azimayi achimasomaso. (2) Ngati Katakwe ali munthudi, wayenera kukhala wachimasomaso. 371