Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 336
Paphata pa Chichewa
mwana ankawasambitsira mu nkhate n’chifukwa chake
amayenda ndi tsoka.
Chitsanzo: Lerotu ndiye mwasambira munkhate.
Sambitsa chokweza: Kuchenjeretsa, kulanga munthu
kapena kumuwonongera chuma.
Chitsanzo: (1) Ngofunika kumusambitsa chokweza. (2)
Osewera mpira a dziko lino asambitsidwa chokweza ndi
osewera a ku Zimbabwe.
Sambula: Nyoza kotheratu, kunena munthu chipongwe.
Chitsanzo: (1) Mayi amene aja amawasambula amuna
awo. Koma m’mawa kukacha, amanyamuka n’kuka-
wasiyira madzi kubafa. (2) Koma ndiye mwandisambulatu!
Sambwadza: Kukalipira, kulalatira munthu.
Chitsanzo: Abwana ake amusambwadza.
Samezamate: Munthu yemwe akayamba kuyankhula
sasiya, wolongolola.
Chitsanzo: Mkazi wake uja ndi samezamate.
Samisoni: Munthu wamphamvu.
Chitsanzo: Anzathu aja anakwatiwa ndi Samisoni.
Samuka: Kuchokapo kupita kwina.
Chitsanzo: Ndikawaona akubwera ndingosamukapo!
Samvamkunkhu: Munthu wopirira amene sathawa nga-
khale amenyedwe.
Chitsanzo: Anyoni ndi samvamkunkhu.
Samvamtsonyo: Munthu amene samasamala ngakhale
anzake azimunyoza.
Chitsanzo: Anasiyani ndi samvamtsonyo, umati
ukawanena, mawa amabwera kwanu kudzapempha
mchere.
Sanatalikire: Sanapite kutali.
Chitsanzo: Adikireni, sanatalikire.
335