Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 256

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Sindingapite kukawaona popanda mituka. Mizu yakachere: Kukumana, kupangana zinazake. Chitsanzo: Amaoneka kuti sagwirizana, koma ndi mizu yakachere. Mjedo (mijedo): Kunena miseche, kunena munthu wina kuseri. Chitsanzo: Mayiwa ndi a mjedo (mijedo). Mkacha: Mawu amenewa ndi dzina la ukonde wamaso aang’ono womwe umakokolola nsomba iliyonse ndi zazing’ono zomwe. Mawuwa amanenedwa ngati munthu watenga matenda kapena wagwera m’mavuto enaake chifukwa cha zochita zake. Chitsanzo: Nawonso anakokololedwa ndi mkacha wa ka- chilombo. Mkamwini wankhanga: Mwamuna wolima kwambiri. Chitsanzo: Pakhomo pano timafuna akamwini ankhanga. Mkangaziwisi: Munthu wosaopa kugwira ntchito ngakhale itakhala yovuta. Chitsanzo: Anthu amene amagwira ntchito kumotchale amakhala a mkangaziwisi. Ena amadyera nsima m’motchale momwemo. Mkango: Munthu wovuta kapena wankhanza. Chitsanzo: Mayi aja anakwatiwa ndi mkango. Amangow- amenya tsiku ndi tsiku. Mkazi wamalonda: Hule, mkazi wachimasomaso, mkazi woyendayenda, mkazi wokonda amuna. Chitsanzo: Mkazi wamalonda anabwera kwawo ndipo amanena kuti akufuna zake. Mkazi wapambali: Mkazi wachiwiri, mkazi wachibwenzi. Chitsanzo: Amuna awo ali ndi mkazi wapambali. 255