Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 243
Paphata pa Chichewa
Matatalazi: Pamakhala mavuto ambiri, si zophweka.
Chitsanzo: Kuti akubwereke ndalama pamakhala
matatalazi.
Matchiki: Mawu omwe achinyamata amanena
akamanena za akazi.
Chitsanzo: Matchiki a masiku ano sayankha ukawapatsa
moni.
Mate: Malovu.
Chitsanzo: (1) Amayankhula ngati m’kamwa mwake
mwadzadza mate. (2) Thawa apa ndikutsira mate.
Matekenya: Matenda odyeka zala zakuphazi.
Muzivala nsapato mungatenge matekenya.
Matenda a boma: Matenda a Edzi.
Chitsanzo: Ukapita kuchipatala mpamene umadziwa kuti
anthu ambiri ali ndi matenda a boma.
Matenda a kayakaya: Matenda oti mwina sachira.
Chitsanzo: Ukaona azimayi akutuluka akumina m’nyum-
ba momwe munali matenda a kayakaya, umangodziwira-
tu kuti zavuta.
Matenda amgonagona: Matenda okhalitsa.
Chitsanzo: Pali anthu ambiri omwe akudwala matenda
amgonagona m’dziko muno.
Matenda akugwa: Matenda a khunyu.
Chitsanzo: Mwanayu ali ndi matenda akugwa.
Matenda osamva mankhwala: Matenda omwe sakuchita
utamwa mankhwala.
Chitsanzo: Matenda awo ndi osamva mankhwala.
Matewe: Miyendo yopindika.
Chitsanzo: Anthu amatewe amakhala amakani.
Matsire: Kudzuka uli wofooka chifukwa cha mowa
womwe unamwa dzulo.
Chitsanzo: Aphikireni phala kuti achotse matsire.
242