Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 175

Paphata pa Chichewa Kupalasa: Kuyenda kwambiri. Chitsanzo: Sindingakwanitse kuyenda nawo limodzi chifu- kwa amapalasa. Kupambana: Kuwina, kukhoza. Chitsanzo: Mwana wanu wapambana mayeso. Kupana: (a) Kukhala pachibwenzi, kufunsira. Chitsanzo: Kodi Jemusi, wapana eti? (b) Kuvulala utaphinyidwa kapena kupanikizidwa ndi chinachake. Chitsanzo: Chitseko chamupana. Kupanda ungwiro: Kukhala munthu wochimwa, kusakhala wangwiro, kukhala munthu wolephera kuchita zinthu bwinobwino. Chitsanzo: Anthu tonse ndi opanda ungwiro. Kupapira: Kumwa madzi kapena mowa mosalekeza. Chitsanzo: Wapapira mabotolo awiri a mowa. Kupata: Kupeza. Chitsanzo: Aulesi sangapate kanthu. Kupatira: Haga, koloweka manja m’khosi mwa wina. Chitsanzo: Muziwakupatira akazi anuwa. Kupenekera: Kunena mosatsimikiza. Chitsanzo: Ndikungopenekera kuti akhoza kukhala anasamuka. Kupepa kwa dzuwa: Kusiya kuwotcha kwambiri, cha- kumadzulo. Chitsanzo: Ndimakonda kuwongola miyendo dzuwa lika- pepa. Kupeputsa: Kunyoza, kuderera. Chitsanzo: (1) Maso amapeputsa kolemera. (2) Sagwiri- zana nanu chifukwa mumamupeputsa. 174