Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 173
Paphata pa Chichewa
Kuonekera ng’amba: Kuonekera poyera.
Chitsanzo: Achinyengo onse aonekera ng’amba.
Kuonera pakhosi: Kutsala pang’ono kumwalira.
Chitsanzo: Moyo tikungoonera pakhosipa.
Kuonerana m’botolo: Kunyozana.
Chitsanzo: Sindidziwa chifukwa chake amaonerana
m’botolo.
Kuonetsa mbwadza: Kukhaulitsa munthu.
Chitsanzo: Anthu olusa amuonetsa mbwadza.
Kuonetsa mfolo: Kuonetsa zoopsa, kuopseza munthu
kuti amumenya. Mawuwa akamauza munthu wina ama-
muuza kuti “udziwa mfolo.”
Chitsanzo: Anzawo awaonetsa mfolo.
Kuonetsa mpeni: Kupha.
Chitsanzo: Mpofunika tambala ameneyu timuonetse
mpeni.
Kuonetsa nyenyezi: Kumenya moopsa moti n’kumaona
ngati nyenyezi.
Chitsanzo: Anzake a mowa anamuonetsa nyenyezi.
Kuonjezera mchere (kuonjezera mchere): Kuonjezera zi-
na.
Chitsanzo: (1) Nkhani zolembedwa chonchi zimakhala zoti
anaonjezeramo mchere. (2) Ndinadziwa kuti nkhaniyi aitsi-
ra mchere.
Kuotcha mtambo: Kupita dziko lina pandege.
Chitsanzo: Chaka chino ndiotcha mtambo.
172