Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 171
Paphata pa Chichewa
Kunyowa: Kuchita manyazi.
Chitsanzo: (1) Koma ndiye mwanyowatu, mpaka
kukalipidwa pamaso pa akazi anu? (2) Mnyamata uja
ndiye wanyowa, zoona kumuyendetsa osavala.
Kunyowa: Kuchita manyazi.
Chitsanzo: Nditayankhula zimenezo ndinanyowa.
Kunyozeka: Kuchita manyazi, kupusa.
Chitsanzo: (1) Koma ndiye anyozekatu mayiwa, kugwa
pagulu ngati pano! (2) Mwanayo anaona bambo ake akun-
yozeka.
Kunyozololoka: Kuonda chifukwa cha matenda kapena
kusowa chakudya m’thupi.
Chitsanzo: Mwanayu mukamapanda kumudyetsa anyozo-
loloka.
Kunyumwa: Kudabwa.
Chitsanzo: Ndainyumwa, n’chifukwa chiyani akundiuza
kuti ndipite ndekha.
Kunyumwitsa: Kuopseza wina.
Chitsanzo: Anyamata aja amandinyumwitsa.
Kunzi: Mphongo.
Chitsanzo: Ntchito zina zimafuna kunzi.
Kuolobza: Kufewetsa.
Chitsanzo: Mate amaolobza shuga kuti akome kwambiri.
Kuoloka moto: Kugonana.
Chitsanzo: Anawapezerera akuoloka moto.
Kuolowa manja: Kukhala munthu wopatsa.
Chitsanzo: Ukakhala woolowa manja, anthu amakuzolow-
era.
170