Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 170
Paphata pa Chichewa
kunyindirira liwiro.
Kunyinduka: Kuphwanyika, kubwanyuka.
Chitsanzo: Nkhumba idagwa ndi chipumi mphuno yake
n’kunyinduka.
Kunyindula:
(a) Mawuwa anganenedwe mwachipongwe ponena za
munthu amene akuyankhula.
Chitsanzo: Sindifuna kuti munthu amene
ndikumuthandiza azinyindulanso pakamwa.
(b) Kuphwanyika pakamwa, kapena kupanyansitsa.
Chitsanzo: Nkhumba inanyinduka kamwa itagwa
mumtengo chifukwa cha dyera.
(c) Mawu onyoza kwambiri onena munthu akamadya
potengera mmene pakamwa pake pakuonekera
makamaka pokudya.
Chitsanzo: Tazingonyindulani nsimayi apa!
Kunyinyirika: Kusafuna kuchita zinazake, kukana
kuchita chinachake, mwano.
Chitsanzo: Ndikamutuma amakonda kunyinyirika.
Kunyong’olera: Kuchotsa zomwe zatsakamira m’kamwa
ukamaliza kudya. Ena amachotsa ndi lilime kapena
kuyendetsayendetsa minofu ya m’kamwa.
Chitsanzo: Amene akunyong’olera wadya kale.
Kunyong’onyeka: Kusowa mtendere, kusaona bwino.
Chitsanzo: Ndikakhala pakhomo ndimanyong’onyeka.
Kunyonyomala: Kunjuta posonyeza ulemu.
Chitsanzo: Mnyamata amafunika azinyonyomala pamaso
pa akulu.
169