Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 161
Paphata pa Chichewa
(c) Kuuza munthu kuti asamangike, azichita zinthu
mopanda mantha.
Chitsanzo: Takulandirani! Khalani omasuka, kuno ndi
kwanu.
(d) Kuyankhula mosabisa mawu.
Chitsanzo: Amati atani, lero lokha ndiye ndawamasula!
Kumasula: Kuuza munthu chilungamo.
Chitsanzo: Lero lokha ndiye ndikumasulani!
Kumata phula m’maso: Kunamiza kapena kupusitsa
munthu.
Chitsanzo: (1) Anandimata phula m’maso kuti amakonza
mafoni, nditangomupatsa, anangolowa m’dzombe
n’kuzimiririka. (2) Mnyamatayo anawamata anthu onse
phula m’maso, powanamiza kuti wachokera kujoni pomwe
ndi wapamtundapa.
Kumbiyazodooka: Kumanda.
Chitsanzo: Masiku ano mitengo yatsala kumbiyazodooka
kokha.
Kumbuyo kulibe maso: Zakumbuyo sizidziwika.
Chitsanzo: Sindingalole kuti ndizidwala m’mimba
chifukwa cha zimene zinachitika chaka chatha. Kumbuyo
kulibe maso!
Kumbwandira: Kugwira.
Chitsanzo: Amumbwandira akuthyola mzimbe m’munda
wa eni.
Kumeneko ndiye kukhala: Mawuwa amanenedwa
pothokoza wina kutanthauza kuti zimene munthuyo
wachita ndi zoyenera kapena zabwino.
160