Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 153
Paphata pa Chichewa
Kulibe manda a mbeta: Mawuwa amatanthauza kuti
n’zotheka kukhala wekha wosakwatira kapena kukwa-
tiwa.
Chitsanzo: Sindidandaula kukhala ndekha, munamva zoti
kuli manda a mbeta!
Kulichete: Kumanda.
Chitsanzo: Mukamva zii ndiye kuti ndatsikira kulichete.
Kulifwafwantha bodza: Kunama kopanda nako manyazi.
Chitsanzo: Atawanamiza makolo athu oyambirira, Satana
analifwafwanthanso bodza lina. Ananena kuti kufa
simudzafa.
Kulikumba liwiro: Kuthamanga kwambiri.
Chitsanzo: Ukaona kuti pathina, umangofunika kulik-
umba liwiro.
Kulilowa banja: Kukwatira kapena kukwatiwa.
Chitsanzo: Anzanutu analilowa banja.
Kulima chidzulo: Kukalima madzulo dzuwa litapepa.
Chitsanzo: Tiyeni tikalime chidzulo.
Kulima pamsana: Kuchenjeretsana, kukhaulitsana.
Chitsanzo: Mabwana anthu ndi amene akutilima pamsa-
na.
Kulimba m’maso: Kusagona msanga.
Chitsanzo: Mwana ameneyu ndi wolimba m’maso.
Kulimba mtima: Kupanda mantha, kusagonja.
Chitsanzo: Ntchito ya ulonda imafuna kulimba mtima.
Kulimba nazo: Kupirira, kuchita khama.
Chitsanzo: Mwana ameneyu ndi wolimba nazo.
152