Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Ngale | Page 23

Ngale Nawonso ogula ngale anakhala m’mawofesi awo n’kumadikirira moleza mtima kuti asodzi abwere kudzagulitsa ngale zawo. Anthu ame- newa anali ochenjera kwambiri chifukwa nsodzi akangofika, ankayamba kumunenerera mpaka agonje. Nsodziyo akakhala watulo ankamugula pamtengo wozizira kwambiri. Ankachita izi kuti nawonso apezepo ke- nakake. Zikuwoneka kuti ngalezi sizinali zawo. Anthuwa anangolem- bedwa ntchito kuti azigula ngale m’mawofesi osiyanasiyana omwe anali m’tawuniyi ndipo bwana wawo anali m’modzi. Choncho si kulakwa kunena kuti asodziwo ankangodzivutitsa akamasankha munthu woti amugulitse ngale zawo chifukwa ogula ngale onse anali amodzi. Ngati pali anthu omwe nkhani ya Kino sikanawaphonya ndiye anali amenewa. Nkhaniyi itangofika m’makutu mwawo, aliyense anayamba kuganizira za tsogolo lake. Onse ankafuna kumuponda n’cholinga choti apeze ndalama zokonzera tsogolo lawo. “Nditangopeza ngale imeneyo,” ankatero mumtima mwawo, “ndikhoza kuyigulitsa n’kutsegula mawofesi angaanga ogula ngale.” Palibe munthu amene sankachita chidwi ndi ngale ya Kino. Aliyense ankafuna kuthetsa mavuto ake ndi ngaleyo ndipo ndi munthu m’modzi yekha amene ankawapingapinga kuti asakwaniritse maloto awowo. Munthu ameneyu anali Kino. Choncho posakhalitsa Kino anakhala mda- ni wa anthu amtima wachikolopawa. Ngaleyi inachitsa kuti tawuni yonse idzadze ndi mdima wa maganizo oyipa komanso achiwembu. Koma Kino ndi mkazi wake sankadziwa zimenezi. Onse anali ndi chisangalalo chophwathula tsaya ndipo ankaganiza kuti aliyense aku- wafunira zabwino. Koma kunena zowona, ndi Juan Tomas yekha ko- manso mkazi wake Apolonia, omwe ankawafuniradi zabwino. Cha- kumadzulo, Kino anakhala pansi m’nyumba mwake n’kumacheza ndi anthu a nyumba zapafupi. Kino anagwira ngale ija m’dzanja lake ndipo inalidi yowoneka bwino zedi. Pamene ankayang’ana ngaleyo, m’mutu mwake munayamba kumveka Nyimbo ya Banja Lake. Ndiyeno Juan Tomas, yemwe anakhala pafupi naye anati, “Ndiye uchita chiyani tsopano? Iwetu watola chikwama!” Kino anayangana ngaleyo ali mwe-e. Nayenso Juana anaphimba 17