Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Ngale 2 | Page 21

Ngale ankakhala ngati akunyalanyaza kuchikanula. Pa nthawiyi, Juana ankangomuyang’ana ndipo kuchedwa kwa mwamuna wakeyo kunkachititsa kuti azingoti mtima phaphapha. Juana anakumbatira Coyotito n’kunena chapansipansi kuti, “Chikanulenitu.” Kino analowetsa mpeni uja pakampata kachikambacho n’kuchikanula. Ngati kutulo, Kino anawona ngale yokongola kwambiri. Inali ngale yamtengo wapatali, moti chibadwireni anali asanawonepo ngale yokon- gola choncho. Ngaleyo inali yayikulu ngati dzira lambalame zamphe- pete mwa nyanja. Juana sankakhulupirira maso ake moti anangoti kakasi, kusowa cho- nena. Kunena zowona, Kino anali ndi chimwemwe chosaneneka. Aka- yang’ana ngaleyo, ankatha kuwona maloto ake onse akukwaniritsidwa. Kenako anatola ngaleyo n’kumayiyang’ana mosamala ndipo anawona kuti inali yopanda chilema chilichonse. Nayenso Juana anabwera pafupi n’kumayang’ana ngaleyo m’dzanja la mwamuna wake. Dzanja limeneli ndi lija anamenya nalo geti ndipo pamene anadzivulaza paja panali patasintha mtundu chifukwa chofewa ndi madzi. Juana anapita pamene anagoneka Coyotito n’kukachotsa masamba anamuyika paphewa aja. “Kino!” anatero Juana. Kino anasiya kaye kuyang’ana ngale ija ndipo anawona kuti phewa la Coyotito layamba kusintha. Zikuwoneka kuti poyizoni uja anali ataya- mba kuchepa mphamvu. Kino anafumbata ngale yake mwamphamvu mumtima mwake mutadzadza chisangalalo chosaneneka. Chisagalalo- cho chinafika posefukira pakamwa pake, moti anakuwa monyadira. Aso- dzi ena, omwe anali pafupi anadabwa ndi zimenezi moti anayamba ku- palasira kumene kunali bwato la Kino. 15