Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 247

Miyambi ya Patsokwe Waba nkhukhu ndamuona, sindimutchula chifukwa choti ndili ndekha. -Mawuwa amatanthauza kuti amene walakwa ndikumudziwa, koma poti palibe amene amagwirizana nane pamudzi pano, sin- ditchula. Wabisa mbuzi m’munda. -Kumeneku ndi kusunga mavuto, mwachitsanzo kusunga waku- ba m’nyumba. Wachaje ndi gaga wowawa, sasipika. -Mawuwa amatanthauza kuti anthu adera amakhala ngati gaga wowawa, yemwe nsima yake sungadye yosipa. Anthu ena amangofuna kuwathandiza basi koma sangakuthandize zitakuvuta. Wachake ndi wachake. -Munthu amene ali ndi khalidwe loipa saleka. Wachake sachileka. -Munthu amene ali ndi khalidwe loipa saleka. Wachedwa ndi makonkhwa. -Makonkhwa ndi zinthu zopanda pake. Mawuwa amanenedwa ngati munthu wina wachedwa chifukwa cha zinthu zopanda pake. Wachenjera atalumwa. -Munthu amachenjera atalumwa kapena kuti atalumidwa ngati anthu ena, kaya alendo, amuchitira chipongwe. Akazindikira chipongwecho amati, “ndachenjera nditalumwa,” zomwe ziku- tanthauza kuti wachenjera zitaipa kale. Wachenjeza ng’anga, chilonda chisanapole. -Mawuwa amanena za sing’anga, kapena kuti dokotala amene akukupatsa mankhwala oti uchire bala lako, koma iweyo 246