Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 246

Miyambi ya Patsokwe Uyenda liti mwana wosayenda nsangawe, utimalizira zam’nk- hokwe. -Kuchita zinthu mwachangu n’kofunika kuopa kuti ntchito idzakupanikize nthawi imodzi. Uyo waona matumbuzi, nyama ndi yake. -Chimene wapeza pogwira ntchito ndiye chako. Si bwino ku- machenjeretsa anthu ena. Matumbuzi ndi mbalame zomwe zim- akonda kudya nyama zakufa, ndiye ngati waona matumbuziwo, nyama imene akufuna kudyayo ndi yako. Uzikhoma chitseko chako kuti anthu apafupi asakhale akuba. -Zimene timachita zingachititse kuti anthu ena akhale okhulupi- rika kapena ayi. Mwachitsanzo, kumangosiya katundu wathu paliponse kungachititse kuti anthu akopeke n’kusanduka akuba. Vuto la Phwiti, akakhuta salawira mtondo. -Pali anthu ena ukawachitira zabwino amangoti zii, osayamikira zimene wawachitira. Amaoneka akakhala kuti akufuna chinachake basi. 245