Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 229

Miyambi ya Patsokwe pamakhala ziyeso zambiri zingakukope kuti uchokepo pabwino- po. Ukakhala wopanda chala usamadane n’kuloza. -Ngati sungathe kugwiritsa ntchito chinthu usamadane ndi ame- ne angathe. Ukakhala wopanda chala, usamadane n’kuloza. -Tisamapondereze mwayi wa anzathu chifukwa choti tilibe. Ukakhala wopanda galu, umalimba ndi mpiringidzo. -Munthu amene alibe galu pakhomo amafunika kukhoma chitseko chake. Kale ankagwiritsa ntchito mtengo kapena kuti mpiringidzo poteteza kuti chitseko chawo chisatseguke chisawa- wa. Tizidalira zimene tili nazo. Ngati tilibe galu, mtengo kapena mwala zingathandize kupirikitsa akuba. Ukakhala wopanda kanthu, dziko umalidyera ku uchi. -Ngakhale munthu wosowa, pa masiku a phwando nayenso amadyako zabwino. Ukakhala wopanda mano usamaswe phale. -Ngati sungathe kugwiritsa ntchito chinthu usamadane ndi ame- ne angathe. Ukakhala wopanda mano, usamaswe phale. -Ifeyo zikatikanika, tisamatsekereze mwayi wa anzathu. Ukakhala wopanda mng’oma umadya mavu. -Munthu amapeza zinthu zogwirizana ndi zomwe ali nazo. Munthu wopanda mng’oma sangadye uchi. Ukakhala wopanda tsitsi, usamabise lumo. -Tisamapondereze anzathu koma tiwapatse mwayi wokhala ndi zomwe akufuna. Ukakhuta pachika, ana apano sakhuta. -Ukakhala ndi zinthu kumasunga chifukwa mawa 228