Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 228

Miyambi ya Patsokwe Ukafuna kupha galu umapezeratu mtengo. -Ndi bwino kupezeratu zinthu zonse zofunika usanayambe kugwira ntchito. Ukaipa dziwa nyimbo. -Palibe munthu amene amadziwa zonse kapena amene ali ndi zonse zofunikira. Zikakuvuta zina umafunika kusakasaka zimene umachita bwino n’kumachita zimenezo. Ukaipa nkhope, dziwa kuvina. -Palibe munthu amene amadziwa zonse kapena amene ali ndi zonse zofunikira. Zikakuvuta zina umafunika kusakasaka zimene umachita bwino n’kumachita zimenezo. Ukaipa nkhope, dziwa nyimbo. -Palibe munthu amene amadziwa zonse kapena amene ali ndi zonse zofunikira. Zikakuvuta zina umafunika kusakasaka zimene umachita bwino n’kumachita zimenezo. Ukakalamba usamabise lumo kuti ena asametere. -Tisamapondereze anzathu koma tiwapatse mwayi wokhala ndi zomwe akufuna. Ukakhala kwa eni umafunika kukhala nkhosa. -Munthu ukakhala kwa eni umayenera kufatsa. Ukamachita matukutuku amakuthamangitsa. Ukakhala m’mwamba usamatukwane pansi, ungadzasowe wokutola ukagwa. -Osamanyoza anzathu tikakhala pabwino. Ukakhala mwana, mphanje umayambira pamchenga. -Ukafuna kuphunzira kuchita zinazake, umafunika kuyamba ndi chophweka. Ukakhala pabwino, poipa pamakuitana. -Mwayi suchedwa kutha. Nthawi zina ukakhala pabwino 227