Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 211
Miyambi ya Patsokwe
kumupatsa zabwino. Ukamupatsa nthuli yabwino amatayira
agalu.
Pondupondu, njira idzera momwemo.
-Zomwe munthu umachitachita zimasanduka chizolowezi. Nga-
ti umachita zoipa zimakulowerera, chimodzimodzi ukamachita
zabwino.
Popanda nkhuni moto sumayaka.
-Nkwiyo uli ngati moto, ukakhazikika pamikangano komanso
kumaputa anzako moto umayaka. Anthu amatha kumenyana
chifukwa chosaugwira mtima.
Potepote mpoyamba, potsiriza ndi chingwe.
-Zinthu zina zimayamba pang’onopang’ono pomaliza n’kukhala
zazikulu. Mwachitsanzo, kuti vuto lichitika, pamakhala kuti pa-
khala pakuchitika zambiri zomwe anthu ankazinyalanyaza.
Psi! luma! n’kukhala ndi mbuyake.
-Mawuwa amanenedwa ngati munthu wina amakonda kudalira
mphamvu za ena.
Pusepuse ulandira mpeni.
-Munthu sukhala wochenjera pa chilichonse, tsiku lina anthu
amakugwira n’kukukhaulitsa.
Pusi adafa m’njakata.
-Tsiku lina pusi ankafuna kugwira zingwe ziwiri nthawi imodzi
moti anasokonezeka n’kugwera pansi moti anathudzuka. Siz-
imatheka kuchita zinthu ziwiri nthawi imodzi. Nthawi zina
umafunika kusankha chimodzi.
210