Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 197

Miyambi ya Patsokwe Odwala agawa mphika. -Mawuwa amanena za munthu amene amakonda kupezeka pamene pali zabwino, osati pamene pali mavuto. Okazinga nthanga akazingira a mano kuti akukute. -Si bwino kuchitira nsanje ena akamathandiza anzawo kuti atukuke. Anthu amachitira zabwino anthu omwe akuoneka kuti ali ndi tsogolo, m’mawu ena ali ndi mano oti akhoza kukukuta. Okoma apitana. -Zabwino zimene timachitira ena zimachititsa kuti ena azitichit- ira zabwino. Okoma atani onga Fungwe. -Anthu ena umatha kuwachitira zabwino koma sayamika. Nya- ma ya Fungwe inali yosowa kwambiri moti ena amati akapatsid- wa nyamayi amathokoza. Tiyenera kumathokoza wina akatikankhira patsogolo. Osachulutsa gaga m’diwa. -Osachulutsa zonena zingasokoneze zinthu. Munthu akaika ga- ga wambiri m’diwa, mbewa imakhutsa isanafike padiwalo. Osagula phazi la Njovu. -Kungoona phazi la njovu sindiye kuti taona njovu. Si bwino kumagula malonda omwe sunawaone. Si bwino kumachita zin- thu mwaphuma komanso mosaganiza bwino. Osamachepetsa kolemera. -Osamaderera zinthu zomwe zingakuthandize. Osamafunsa chinyezi kubafa. -Mawuwa amanena za munthu amene akufunsa zinthu zoti aku- zidziwa kale. Nanga ndi ndani amene angakhale pansi n’kuma- funsa ngati kubafa kumakhala chinyezi kapena ayi? 196