Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 183

Miyambi ya Patsokwe anthuanthu, ofooka sangazithe. Ngati n’zotheka kuwapha ndi uchi, n’chifukwa chiyani ukufu- na kuwapha ndi chiphe? -Kumagwiritsa ntchito njira imene ukuona kuti ndi yabwino kwambiri. Ngati umakonda bwenzi lako, usamubwereke ndalama. -Nthawi zambiri nkhani za ndalama zimachititsa kuti anthu asi- yane. Tizisamala pa nkhani yobwereka ena ndalama. Ngati munthu timagwirizana naye kwambiri, tingachite bwino osamubwereka ndalama chifukwa akhoza kungotikhumud- witsa. Ngongole imakoma potenga, koma pobweza imawawa. -Ukamatenga ngongole zimasangalatsa koma kuti ubweze pa- makhala nkhani. Tiziganiza kaye tisanatenge ngongole. Nguluwe inalira nsampha utaning’a. -Nguluwe itagwidwa pansampha analimbana nawo mpaka kutsala pang’ono kuduka. Koma m’malo molimbikira inatopa ndipo inayamba kulira. Anthu atamva kulirako anabwera n’kud- zaipha. Osamataya mtima msanga tikakhala pamavuto. Nguluwe ya ana sinona. -Nguluwe imene yabereka ana ambiri imakhala yoonda. Chimodzimodzinso ndi munthu yemwe ali ndi ana ambiri kapena amene amamudalira ambiri. Chifukwa ndalama zake zimachuluka kopita, satukuka. Tizikhala ndi ana omwe tingakwanitse kuwasamalira. Nguwo yobwereka siilimba m’thupi. -Nguwo ndi nsalu. Nsalu yobwereka simachedwa kugwa chifu- kwa umakhala sunaizolowere. Tisamadalire za ena, tizipeza za- thu. 182