Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 147

Miyambi ya Patsokwe Mkazi wa mfumu akati mlomo tololo, wataya mudzi. -Ngati mkazi wa mfumu ndi wolongolola, zinthu zimasokon- ekera m’mudzi. Koma akakhala wofatsa zinthu zimayenda bwino. Mkazi wa mfumu asamati khutu petupetu. -Mkazi wa mfumu asamakhale wamabodza chifukwa akhoza kunamiza mwamuna wake n’kupasula mudzi. Mkazi wa mtsogoleri ayenera kukhala wodziletsa. Mkazi wabwino amaphika nsima yosazizira. -Mkazi akamalandira bwino alendo, zimachititsa kuti mwamuna wake akadzipita koyenda anthu adzamuphikire nsima. Zikatere nsima anaphika mkazi wake ija imakhala ngati sinazizire. Mkazi wophika msima yosazizira. -Mawuwa amanenedwa potamanda mkazi amene amalandira bwino alendo powaphikira chakudya chabwino. Mwamuna wakenso amalandiridwa bwino akapita kwa anzake, m’mawu ena nsima imene anaphika ija imakhala ngati ikutenthabe. Mkhalamba msana, usiku ndi kamnyamata. -Maonekedwe amapusitsa. Anthu ena amaoneka abwino pa- maso, koma kuseri ali zilombo. Mkoma akadadza. -Pali anthu ena omwe amaonetsa makhalidwe abwino akakhala kuchilendo, koma akakhazikika amayamba kuonetsa mawanga awo enieni. Mkuntho umodzi supha njoka. -Pofuna kuchita zinthu pamafunika khama, osati kungochita ka- modzi kokha. Mwachitsanzo, ngati ukufuna kulangiza munthu kuti asiye khalidwe loipa, umayenera kuchita khama, apo ayi njoka imene ili mwa iye singafe. 146