Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 146

Miyambi ya Patsokwe Choncho, tiyenera kuonetsetsa kuti tikuwachitira zabwino. Chimodzimodzinso pantchito. Mkamwini wankhuli adathira thendo la inswa pansanamira. -Tiziyamba taonetsetsa tisananyanyale kuchita zinthu, chifukwa nthawi zina tikanyanyala timataya zabwino. Mkamwini waumbombo anakabisa mtolo wa mapira kumadzi. -Tikakhala ndi zinthu ndi bwino kumagawirako ena chifukwa tikapanda kutero zimawonongeka. Mkanda wako ndi umene uli pakhosi. -Timafunika kumakhutira ndi zomwe tili nazo. Mkango ukazingwa umadya udzu. -Ukakhala pamavuto susankha, kunyada umakusiya kaye apo, n’kuyesetsa kuchita chilichonse kuti uthandizike. Mkazi m’modzi diso limodzi, akazi awiri maso awiri. -Munthu ukakhala pamitala sukhala pamavuto kwambiri ngati mkazi m’modzi wamwalira. Mwambiwu umatanthauza kuti ukakhala ndi podalira pawiri suvutika kwenikweni pamodzi pa- kavuta. Mkazi mmodzi ndi diso lopsinya. -Si bwino kudalira chinthu chimodzi, chifukwa zikavuta umasowa pogwira. Mkazi ndi chitenje, chimathera pakhomo. -Mkazi amayenera kukhala pakhomo n’kumasamalirapo bwino. Mkazi si m’bale wako. -Nthawi zambiri ukakwatira umakonda kwambiri mkazi wako. Ena amafika pomanyoza achibale. Koma banja likatha limawa- wasa kwambiri moti anthu ake amafika polakalaka wina at- amwalira kuti asadzamuonenso. Chikondi chimatha banja lika- tha. 145