Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 138

Miyambi ya Patsokwe Mbalame ikakula siikhala paphira. -Munthu wamkulu ayenera kukhala ndi khalidwe, monga mun- thu wamkulu osati ngati mwana. Mbalame ikatera pauta silasika. -Kumakhala kovuta kuti uweruze mlandu wa m’bale wako mak- amaka akapezeka kuti iyeyo ndi amene ali wolakwa. Mbalame yagwa pa uta. -Zinthu zavuta, zimakhala kuti zavuta basi. Mbalame yakwawo ndi yakwawo, siiwala kwawo. -Palibe angaiwale kwawo ngakhale kutakhala kutali bwanji. Mbalame yamchira imamveka ikalira. -Munthu waluso amadziwika ndi zimene amachita. Mbalame zamthenga zofanana zimamwera chigoba chimodzi. -Anthu ochita zofanana amayendera limodzi. Mbalame zofanana nthenga zimayendera limodzi. -Anthu ochita zofanana amayendera limodzi. Mbalame zomwera chigoma chimodzi zimadziwana mthenga. -Anthu a khalidwe lofanana amadziwana komanso kuchitira zinthu limodzi. Mbaliwali idabutsa chimoto. -Zinthu zazing’ono zikhoza kuyambitsa mavuto aakulu ngati mmene kamoto kakang’ono kamayambitsira chomoto chachiku- lu n’kuotcha nkhalango yonse. Mbawala siimwa madzi Galu ali kumbuyo. -Munthu sangachite bwino chinthu, anthu ena akamamusowetsa mtendere. Mbawala yamantha idapota nyanga. -Mantha amapulumutsa, umapewa mavuto omwe 137