Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 137

Miyambi ya Patsokwe Mawu okweza ndawamva, am’munsi ndi nkhondo. -Mawu abwino amawakweza, oipa amawang’ung’udza kuti ena asamve. Mawu osiyiza adaombola Kalulu. -Nthawi zina anthu akatifunsa kuti tifotokoze nkhani tiyenera kukamba nkhani modzigwira, osangonena chilichonse pokhapo- kha ngati pakufunika kutero. Mawu oswera mpanje (ng’oma) adautsa Fisi. -Pakakhala mlandu ndi bwino kungonena zolakwazo, koma ukayamba kufotokoza zidani zimene zinalipo kale, umatosa zambiri. Mawu oyamba anaphetsa Kalulu. -Munthu ukafuna kuti umve zambiri umafunika kukhala woleza mtima, osamangotengeka ndi zinthu zomwe sunazimvetse. Mawu salawa, amalawa ndi chakudya. -Osamayankhula moyerekeza ngati ukuwalawa kaye. Mayankhayankha a pabwalo anatalikitsa Sakhwi mlomo. -Poyankhula tizisamala, osamangochulukitsa mawu osafunika. Mayendayenda amapha mapazi. -Kuyendayenda kapena kuthamangathamana kumabweretsa mavuto mwinanso imfa. Anthu amatha kumwalira chifukwa mapazi awo anawatengera malo olakwika. Mayendayenda amapha miyendo. -Kuyendayenda kapena kuthamangathamanga kumabweretsa mavuto nthawi zina. Mbalame ikakhala pauta silasika. -Zimakhala zovuta kuweruza mlandu wa m’bale wako. 136