Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 135

Miyambi ya Patsokwe Mawere awirirana. -Mawuwa amanenedwa ngati anthu apachibale sakugwirizana. Mawere kapena kuti mabere amafunika kumakhala limodzi pamtima, koma ngati atakula kwambiri amayamba kupaniki- zana. Mawonekedwe amapusitsa. -Zinthu zina zimangokongola m’maonekedwe pomwe si zokon- gola kwenikweni. Mawu a akulu amakoma akagonera. -Mawu a akulu amakumbukiridwa pakapita nthawi ndiponso pamene zomwe amanena zachitikadi. Mawu a akulu amakoma akagonera. -Mawu amene munthu wamkulu wanena amadzaoneka kuti anali othandiza pakapita nthawi. Ndi bwino kumawatsatira. Mawu a chitsiru amakoma akagonera. -Mawu onenedwa ndi munthu wooneka ngati wopusa amadza- khala othandiza m’tsogolo. Si bwino kumanyoza malangizo a anthu ooneka monyozeka chifukwa nthawi zina amakhala othandiza. Mawu a munthu m’modzi ndi chisa cha njuchi. -Ndi bwino kufunsa ena ukamva zinazake m’malo mofunsa m’modzi chifukwa nthawi zina amangooneka okoma koma liri bodza. Mawu abwino saiwalika. -Mawu oona samalephereka, amachitikadi. Komanso mawu abwino, omwe munthu wanena amakumbukiridwa kwa nthawi yaitali. Mawu akuseri. -Mawu achinsinsi. Anthu amanena mawu amenewa m’malo 134