Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 134

Miyambi ya Patsokwe Matumbo a Nkhuku amafinyidwa paokha. -Osamadzitama pagulu chifukwa tsiku lina zoipa zako zimadzaululika n’kuipitsa mbiri yako yonse. Matupa akumana. -Anthu amakani okhaokha akakumana sakuna kugonjerana pokhapokha wina awalanditse. Maungu amafuwa pali moto. -Amenewa ndi mawu amene anthu amanena mwana wa makolo abwino akakhala wamakhalidwe oipa. Maungu kubalira kumphuno. -Mawawa amanenedwa munthu akamadandaula kuti zabwino zabwera mochedwa. Mavu anapangana kuning’a pamimba. -Ndi bwino kumachita zinthu mogwirizana. Ngakhale kuti pan- gano limavuta kusunga nthawi zina, komabe tiziyesetsa kusunga zomwe tagwirizana popewa kukhumudwitsa ena. Mavuto saona nkhope. -Aliyense kaya ndi wabwino, wokongola kaya wotani, ama- kumana ndi mavuto. Mavuto sasowa. -Kulikonse kumapezeka mavuto, palibe angawathawe. Mavuto si maliro okha. -Pali zinthu zina zomwe zimasowetsa mtendere kwambiri ngati imfa, monga kusamvera kwa ana komanso zina. Mawa ndi lero lomwe. -Mwambiwu anthu amaunena popempha ngati kunena kuti ndi bwino mungondibwereka chifukwa mawa ndi lero lomwe, si kalekale. 133