Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 118

Miyambi ya Patsokwe kuyambira limodzi ndi anzako. Liwiro lilibe manyazi, chikakula patuka. -Sitingathe kulimbana ndi Njovu ikakalipa. Tiyenera kungothawa basi. Si bwino kumayesetsa kuchita zinthu zomwe tikudziwa bwino kuti sizingatheke. Lonjezo linadulitsa mutu wa Yohane. -Uyenera kukwaniritsa zimene walonjeza. Lungalunga mpobadwa, chilema chidza ku usana. -Munthu ukhoza kulumala utakula kale. Munthu akhoza kubad- wa ali bwinobwino n’kukhala ndi chilema atakula kale chifukwa cha matenda kapena ngozi. Ungatanthauzenso kuti munthu ukhoza kuyamba bwino koma pamapeto pake n’kusokoneza zinthu. Lungalunga mpobadwa, chilema chimadza utakula. -Munthu ukhoza kulumala utakula kale. Ungatanthauzenso kuti munthu ukhoza kuyamba bwino koma pamapeto pake n’kusokoneza zinthu. 117