Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 117

Miyambi ya Patsokwe Lero zakumana mbombo zokhazokha. -Anthu a makhalidwe ofanana akakumana pamakhala mavuto, palibe angapusitse mnzake. Likawomba wotheratu. -Mwayi ukapezeka, kapenanso ukakhala ndi nthawi, mpofunika kuchitiratu zomwe ukufuna kuchita, chifukwa mwina tsiku lotsatira kudzakhala mitambo. Si bwino kumachita zinthu mochedwa mwayi ukapezeka. Ndi bwino kumachitiratu zinthu mwayi ukadalipo. Linda madzi apite, kenako uziti “ndadala.” -Osamapupuluma kunena kuti zinthu zili bwino, chifukwa pamapeto pake ukhoza kupusa utakumana ndi mavuto. Si bwino kudzitama vuto lisanathe. Linda mphepo iwombe kuti uone maliseche a Nkhuku. -Pakagwa mavuto m’pamene umadziwa khalidwe lenileni la mnzako. Lirime ndi nkhondo. -Mawu akhoza kuyambitsa nkhondo. Ndi bwino kumaganiza kaye tisanayankhule kuopera kubweretsa mavuto titayankhula zopanda nzeru. Liuma lidakumbitsa Mbewa zapachulu. -Nthawi zina makani amachititsa kuti uvutike kwambiri. Mwachitsanzo, kuti munthu ukumbe mbewa zapachulu umafu- nika kukhala ndi mphamvu. Ngati munthu ukufuna kuchita chinthu monga kukumba mbewa zapachulu, uyenera kuchita khama. Kusamva kungachititse kuti munthu akumbebe mbe- wazi n’kukhaula. Liwiro la mumchenga n’kuyambira limodzi. -Ngati ukufuna kuti zinthu zikuyendere bwino, ndi bwino 116